Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 13:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Pakuti ife tidziwa mderamdera, ndimo tinenera mderamdera.

10. Koma pamene cangwiro cafika, tsono camderamdera cidzakhalacabe.

11. Pamene ndinali mwana, ndinalankhula ngati mwana, ndinalingirira ngati mwana, ndinawerenga ngati mwana; tsopano ndakhala munthu, ndayesa cabe zacibwana.

12. Pakuti tsopano tipenya m'kalirole, ngati cimbuuzi; koma R pomwepo maso ndi maso. Tsopano ndizindikira mderamdera; koma pomwepo ndidzazindikiratu, monganso ndazindikiridwa.

13. Ndipo tsopano zitsala cikhulupiriro, dyembekezo, cikondi, zitatu izi; koma cacikuru ca izi ndico cikondi.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 13