Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 12:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Pakutinso thupisilikhala ciwalo cimodzi, koma zambiri.

15. Ngati phazi likati, Popeza sindiri dzanja, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

16. Ndipo ngati khutu likati, Popeza sindiri diso, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

17. Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?

18. Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m'thupi, monga anafuna.

19. Koma ngati zonse zikadakhala ciwalo cimodzi, likadakhala kuti thupi?

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 12