Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 12:10-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. ndi kwa wina macitidwe a mphamvu; ndi kwa wina cinenero; ndi kwa wina cizindikiro ca mizimu; kwa wina malilime a mitundu mitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

11. Koma zonse izi acita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense payekha monga afuna.

12. Pakuti monga thupi liri limodzi, nilikhala nazo ziwalo zambiri; koma ziwalo zonse za thupilo, pokhala zambiri, ziri thupi limodzi; momwemonso Kristu.

13. Pakutinso mwa Mzimu mmodzi ife tonse rinabatizidwa kulowa m'thupi limodzi, ngakhale Ayuda, ngakhale Ahelene, ngakhale akapolo, ngakhale mfulu; ndipo tonse tinamwetsedwa Mzimu mmodzi.

14. Pakutinso thupisilikhala ciwalo cimodzi, koma zambiri.

15. Ngati phazi likati, Popeza sindiri dzanja, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

16. Ndipo ngati khutu likati, Popeza sindiri diso, sindiri wa thupi; kodi siliri la thupi cifukwa ca ici?

17. Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?

18. Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m'thupi, monga anafuna.

19. Koma ngati zonse zikadakhala ciwalo cimodzi, likadakhala kuti thupi?

20. Kama tsopano pali ziwalo zambiri, kama thupi limodzi.

21. Ndipo dise silingathe kunena kwa dzanja, Sindikufuna iwe, kapenanso mutu kwa mapazi, Sindikufunani inu.

22. Koma makamakatu ziwalozo zoyesedwa zofoka m'thupi, zifunika;

23. ndipo zimene tiziyesa Zocepa ulemum'thupi, pa izi tiika ulemu wocuruka woposa; ndi zinthu zosakoma zikhala naco cokometsera coposa,

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 12