Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 10:5-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.

6. Koma zinthu izi zinacitika, zikhale zoticenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.

7. Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.

8. Kapena tisacite dama monga ena a iwo anacita dama, nagwa tsiku limodzi zikwi makumi awiri ndi zitatu.

9. Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.

10. Kapena musadandaula, monga ena a iwo anadandaula, naonongeka ndi woonongayo.

11. Koma izi zinacitika kwa iwowa monga zoticenjeza, ndipo zinalembedwa kuticenjeza ife, amene matsirizidwe a nthawi ya pansi pano adafika pa ife.

12. Cifukwa cace iyewakuyesa kuti ali ciriri, ayang'anire kuti angagwe,

13. Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

14. Cifukwa cace, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.

15. Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu cimene ndinena.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 10