Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 10:13-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.

14. Cifukwa cace, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.

15. Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu cimene ndinena.

16. Cikho ca dalitso cimene tidalitsa, siciri ciyanjano ca mwazi wa Kristu kodi? Mkate umene tinyema suli ciyanjano ca thupi la Kristu kodi?

17. Pakuti mkate ndiwo umodzi, cotero ife ambiri ndife thupi limodzi; pakuti ife tonse titengako ku mkate umodzi.

18. Tapenyani Israyeli monga mwa thupi; kodi iwo akudya nsembezo alibe ciyanjano ndi guwa la nsembe?

19. Ndinena ciani tsono? kuti coperekedwa nsembe kwa mafano ciri kanthu? Kapena kuti fane liri kanthu kodi?

20. Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda.

21. Simungathe kumwera cikho ca Ambuye, ndi cikho ca ziwanda; simungathe kulandirako ku gome la Ambuye, ndi ku gome la ziwanda.

22. Kapena kodi ticititsa nsanje Ambuye? Kodi mphamvu zathu ziposa iye?

23. Zinthu zonse ziloleka; koma sizipindula zonse. Zinthu zonse ziloleka; koma sizimanga zonse.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 10