12. Cifukwa cace iyewakuyesa kuti ali ciriri, ayang'anire kuti angagwe,
13. Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.
14. Cifukwa cace, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.
15. Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu cimene ndinena.