Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 10:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti sindifuna, kuti mukhale osadziwa, abale, kuti makolo athu onse anali pansi pa mtambo, naoloka nyanja onse;

2. nabatizidwa onse kwa Mose, mumtambo, ndi m'nyanja,

3. nadya onse cakudya cauzimu cimodzimodzi;

4. namwa onse cakumwa cauzimu cimodzimodzi; pakuti anamwa mwa thanthwe lauzimu lakuwatsata; koma thanthwelo ndiye Kristu.

5. Koma ocuruka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'cipululu.

6. Koma zinthu izi zinacitika, zikhale zoticenjeza ife, kuti tisalakalake zoipa ife, monganso iwowo analakalaka.

7. Kapena musakhale opembedza mafano, monga ena a iwo, monga kwalembedwa, Anthu anakhala pansi kudya ndi kumwa, nanyamuka kusewera.

8. Kapena tisacite dama monga ena a iwo anacita dama, nagwa tsiku limodzi zikwi makumi awiri ndi zitatu.

9. Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.

10. Kapena musadandaula, monga ena a iwo anadandaula, naonongeka ndi woonongayo.

11. Koma izi zinacitika kwa iwowa monga zoticenjeza, ndipo zinalembedwa kuticenjeza ife, amene matsirizidwe a nthawi ya pansi pano adafika pa ife.

12. Cifukwa cace iyewakuyesa kuti ali ciriri, ayang'anire kuti angagwe,

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 10