Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 1:26-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Pakuti penyani maitanidwe anu, abale, kuti 3 saitanidwa ambiri anzeru, monga mwa thupi; ambiri amphamvu, mfulu zambiri, iai;

27. koma 4 Mulungu anasankhula zopusa za dziko lapansi, kuti akacititse manyazi anzeru; ndipo zofoka za dziko lapansi Mulungu anazisankhula, kuti akacititse manyazi zamphamvu;

28. ndipo zopanda pace za dziko lapansi, ndi zonyozeka, anazisankhula Mulungu, ndi zinthu zoti kulibe; 5 kuti akathere zinthu zoti ziriko;

29. 6 kuti thupi liri lonse lisadzitamande pamaso pa Mulungu.

30. Koma kwa iye muli inu mwa Kristu Yesu, 7 amene anayesedwa kwa ife nzeru ya kwa Mulungu, ndi cilungamo ndi ciyeretso ndi ciombolo;

31. kuti monga mwalembedwa, iye amene adzitamanda, adzitamande mwa Ambuye.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 1