Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 8:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova wa makamui anadza kwa ine, ndi kuti,

2. Atero Yehova wa makamu: Ndimcitira nsanje Ziyoni ndi nsanje yaikuru, ndipo ndimcitira nsanje ndi ukali waukuru.

3. Atero Yehova: Ndabwerera kudza ku Ziyoni, ndidzakhala pakati pa Yerusalemu; ndi Yerusalemu adzachedwa, Madzi wa coonadi; ndi phiri la Yehova wa makamu, Phiri lopatulika.

4. Atero Yehova wa makamu: M'miseu ya Yerusalemu mudzakhalanso amuna ndi akazi okalamba, yense ndi ndodo yace m'dzanja lace cifukwa ca ukalamba wace.

5. Ndi m'miseu ya mudzi mudzakhala ana amuna ndi akazi akusewera m'miseu yace.

6. Atero Yehova wa makamu: Cikakhala codabwitsa pamaso pa otsala a anthu awa masiku awo, kodi cidzakhalanso codabwitsa pamaso panga? ati Yehova wa makamu.

7. Atero Yehova wa makamu: Taonani, ndidzapulumutsa anthu anga m'dziko la kum'mawa, ndi m'dziko la kumadzulo;

8. ndipo ndidzabwera nao, nadzakhala m'kati mwa Yerusalemu; ndipo iwo adzakhala anthu anga, nanenso ndidzakhala Mulungu wao, m'coonadi ndi m'cilungamo.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 8