Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 7:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunacitika caka cacinai ca mfumu Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya tsiku lacinai la mwezi wacisanu ndi cinai, ndiwo Kisilevi.

2. Ndipo a ku Beteli anatuma Sarezere ndi Regemeleke ndi anthu ao, apepeze Yehova,

3. nanene kwa ansembe a nyumba ya Yehova wa makamu, ndi kwa aneneri, ndi kuti, Kodi ndilire mwezi wacisanu, ndi kudzipatula, monga umo ndikacitira zaka izi zambiri?

4. Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,

5. Nena kwa anthu onse a m'dziko, ndi kwa ansembe, kuti, Muja mukasala ndi kulira mwezi wacisanu, ndi wacisanu ndi citatu, zaka izi makumi asanu ndi awiri, kodi mukasalira Ine, Inedi?

Werengani mutu wathunthu Zekariya 7