Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 4:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pamenepo ndinayankha, ndinati kwa iye, Mitengo iyi iwiri ya azitona kulamanja ndi kulamanzere kwa coikapo nyali nciani?

12. Ndipo ndinayankha kaciwiri, ndinati naye, Nzotani nthambi ziwiri izi za azitona zirikutsanula zokha mafuta onga golidi mwa misiwe iwiri yagolidi?

13. Ndipo anandiyankha, nati, Sudziwa kodi kuti nziani izi? Ndipo ndinati, Iai, mbuyanga.

14. Pamenepo anati, Awa ndi ana amuna awiri a mafuta oimirira pamaso pa Mbuye wa dziko lonse lapansi.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 4