Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 14:8-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo kudzacitika tsiku lomwelo kuti madzi amoyo adzaturuka ku Yerusalemu; gawo lao lina kumka ku nyanja ya kum'mawa, ndi gawo lina kumka ku nyanja ya kumadzulo; adzatero nyengo ya dzinja ndi ya mwamvu.

9. Ndipo Yehova adzakhala mfumu ya dziko lonse; tsiku lomwelo Yehova adzakhala Iye yekha, ndi dzina lace ilo lokha.

10. Dziko lonse lidzasandulika, lidzanga cidikha, kuyambira ku Geba kufikira ku Rimoni, kumwela kwa Yerusalemu; ndipo pali uwupo padzakhala ponyamuka, ndipo udzakhala m'malo mwace, kuyambira ku cipata ca Benjamini kufikira ku malo a cipata coyamba, kufikira ku cipata ca kungondya, ndi kuyambira nsanja ya Hananeli kufikira ku zoponderamo mphesa za mfumu.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 14