Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 14:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo banja la ku Aigupto likapanda kukwera, losafika, sirdzawagwera kodi mliri umene Yehova adzakantha nao amitundu osakwera kusunga madyerero amisasa?

19. Ili ndi cimo la Aigupto, ndi cimo la amitundu onse osakwerako kusunga madyerero a misasa.

20. Tsiku lomwelo padzaoneka pa miriu ya akavalo OPATULIKIRA YEHOVA; ndi mbiya za m'nyumba ya Yehova zidzanga mbale za ku guwa la nsembe.

21. Inde mbiya zonse za m'Yerusalemu ndi m'Yuda zidzakhala zopatulikira Yehova wa makamu; ndi onse akuphera nsembe adzafika nadzatengako, ndi kuphikamo; ndipo tsiku lomwelo simudzakhalanso Mkanani m'nyumba ya Yehova wa makamu.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 14