Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 12:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tsiku lomwelo kudzakhala maliro akuru m'Yerusalemu, ngati maliro a Hadadirimoni m'cigwa ca Megidoni,

12. Ndipo dziko lidzalira, banja liri lonse pa lokha; banja la nyumba ya Davide pa lokha, ndi akazi ao pa okha; banja la nyumba ya Natani pa lokha, ndi akazi ao pa okha;

13. banja la nyumba ya Levi pa lokha, ndi akazi ao pa lokha; banja la Asimei pa okha, ndi akazi ao pa okha;

14. mabanja onse otsala, banja liri lonse pa lokha, ndi akazi ao pa okha.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 12