Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 11:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsegula pa makomo ako Lebano, kuti moto uthe mikungudza yako.

2. Cema, mtengo wamlombwa, pakuti mkungudza wagwa, popeza mitengo yokoma yaipitsidwa; cemani athundu a ku Basani, pakuti nkhalango yocinjirizika yagwa pansi.

3. Mau a kucema kwa abusa! pakuti ulemerero wao waipsidwa; mau a kubangula kwa misona ya mikango! pakuti kudzikuza kwa Yordano kwaipsidwa.

4. Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;

5. zimene eni ace azipha, nadziyesera osaparamula; ndi iwo akuwagulitsa akuti, Alemekezedwe Yehova, pakuti ine ndine wolemera; ndi abusa ao sazicitira cifundo.

6. Pakuti sindidzacitiranso cifundo okhala m'dzikomo, ati Yehova; koma taonani, ndidzapereka anthu, yense m'dzanja la mnansi wace, ndi m'dzanja la mfumu yace; ndipo iwo adzakantha dzikoli, ndi m'dzanja mwao sindidzawalanditsa.

7. M'mwemo ndinadyetsa zoweta zakukaphedwa, ndizo zoweta zonyankhalala. Ndipo ndinadzitengera ndodo ziwiri; yina ndinaicha Cisomo, inzace ndinaicha Comanganitsa; ndipo ndinadyetsa zowetazo.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 11