Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 11:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsegula pa makomo ako Lebano, kuti moto uthe mikungudza yako.

2. Cema, mtengo wamlombwa, pakuti mkungudza wagwa, popeza mitengo yokoma yaipitsidwa; cemani athundu a ku Basani, pakuti nkhalango yocinjirizika yagwa pansi.

3. Mau a kucema kwa abusa! pakuti ulemerero wao waipsidwa; mau a kubangula kwa misona ya mikango! pakuti kudzikuza kwa Yordano kwaipsidwa.

4. Atero Yehova Mulungu wanga: Dyetsani zoweta zakukaphedwa;

Werengani mutu wathunthu Zekariya 11