Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zekariya 1:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MWEZI wacisanu ndi citatu, caka caciwiri ca Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido mneneri, ndi kuti,

2. Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.

3. Cifukwa cace uziti nao, Atero Yehova wa makamu: Bwererani kudza kwa Ine, ati Yehova wa makamu, ndipo Ine ndidzabwerera kudza kwa inu, ati Yehova wa makamu.

4. Musamakhala ngati makolo anu, amenie aneneri akale anawapfuulira, nd kuti, Atero Yehova wa makamu Bwereranitu kuleka njira zanu zoipa, ndi macitidwe anu oipa; ko ma sanamva, kapena klimvera Ine ati Yehova.

5. Makolo anu, ali kut iwowo? ndi alieneri, akhala nd moyo kosatha kodi?

6. Koma mau anga ndi malemba anga, amene ndinalamulira atumiki anga aneneriwo, kodi sanawapeza makolo anu? ndipo anabwera, nati, Monga wno Yehova wa makamu analingirira kuticitira ife, monga mwa njira zathu ndi monga mwa macitidwe athu, momwemo anaticitira. Masomphenya oyamba: akavalo,

7. Tsiku la makumi awiri ndi cinai la mwezi wakhumi ndi cimodzi, ndiwo mwezi wa Segati, caka caciwiri ca Dariyo, mau a Yehova anadza kwa Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido mneneri, ndi kuti,

8. Ndinaona usiku, taonani, munthu woyenda pa kavalo wofiira, alikuima pakati pa mitengo yamcisu inali kunsi; ndi pambuyo pace panali akavalo ofiira, odera ndi oyera.

9. Pamenepo ndinati, Awa ndi ciani, mbuyanga? Ndi mthenga wakulankhula ndi ine anati kwa ine, Ndidzakuonetsa awa ndi ciani.

10. Ndipo wakuima pakati pa mitengo yamcisu anayankha, nati, Awa ndiwo amene Yehova anawatumiza ayendeyende m'dziko.

Werengani mutu wathunthu Zekariya 1