Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zefaniya 3:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka uyo wopanduka, ndi wodetsedwa, ndiye mudzi wozunza!

2. Sanamvera mau, sanalola kulangizidwa; sanakhulupirira Yehova, sanayandikira kwa Mulungu wace.

3. Akalonga ace m'kati mwace ndiwo mikango yobangula; oweruza ace ndi mimbulu ya madzulo, sasiya kanthu ka mawa.

4. Aneneri ace ndiwo anthu a matukutuku ndi onyenga; ansembe ao anaipsa malo opatulika, napotoza cilamulo.

5. Yehova pakati pace ali wolungama; sadzacita cosalungama, m'mawa ndi m'mawa aonetsera ciweruzo cace poyera, cosasowa kanthu; koma wosalungama sadziwa manyazi.

Werengani mutu wathunthu Zefaniya 3