Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Zefaniya 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Yehova amene anadza kwa Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya, masiku a Yosiya, mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.

2. Kuzitha ndidzazitha zonse kuzicotsa panthaka, ati Yehova.

3. Ndidzatha munthu ndi nyama; ndidzatha mbalame za m'mlengalenga, ndi nsomba za m'nyanja, ndi zokhumudwitsa pamodzi ndi oipa; ndipo ndidzaononga anthu kuwacotsa panthaka, ati Yehova.

4. Ndipo ndidzatambasulira dzanja langa pa Yuda, ndi pa onse okhala m'Yerusalemu; ndipo a ndidzaononga otsala a Baala kuwacotsa m'malo muno, ndi dzina la Akemari pamodzi ndi ansembe;

Werengani mutu wathunthu Zefaniya 1