Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoweli 1:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Yehova a kwa Yoeli mwana wa Petueli.

2. Imvani ici, akulu akulu inu, nimuchere khutu, inu nonse okhala m'dziko. Cacitika ici masiku anu kodi, kapena masiku a makolo anu?

3. Mufotokozere ana anu ici, ndi ana anu afotokozere ana ao, ndi ana ao afotokozere mbadwo wina.

4. Cosiya cimbalanga, dzombe lidacidya; ndi cosiya dzombe, cirimamine adacidya; ndi cosiya cirimamine, anoni adacidya.

5. Galamukani, oledzera inu, nimulire; bumani, nonse akumwa vinyo, cifukwa ca vinyo watsopano; pakuti waletsedwa pakamwa panu.

6. Pakuti mtundu wadza, wakwerera dziko langa, wamphamvu wosawerengeka, mano ace akunga mano a mkango, nukhala nao mano acibwano a mkango waukuru.

7. Unaonongadi mpesa wanga, nunyenya mkuyu wanga, nuukungudza konse, nuutaya; nthambi zace zasanduka zotumbuluka.

Werengani mutu wathunthu Yoweli 1