Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 9:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo zinamuka kwa Yoswa kumisasa ku Giligala, niziti kwa iye ndi kwa amuna a Israyeli, Tacokera dziko lakutali, cifukwa cace mupangane nafe.

7. Ndipo amuna a Israyeli anati kwa Ahivi, Kapena mulimkukhala pakati pa ife, ndipo tipanganenji ndi inu?

8. Koma anati kwa Yoswa, Ndife akapolo anu. Pamenepo Yoswa anati kwa iwo, Ndinu ayani? ndipo mufuma kuti

9. Ndipo anati kwa iye, Akapolo anu afumira dziko la kutalitali, cifukwa lea dzina la Yehova Mulungu wanu; pakuti tidamva mbiri yace, ndi zonse anacita m'Aigupto,

10. ndi zonse anacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni, ndi Ogi mfumu ya ku Basana wokhala ku Asitorotu.

11. Ndipo akuru athu ndi nzika zonse za m'dziko mwathu zidanena nafe ndi kuti, Mutenge m'dzanja lanu kamba wa paulendo, kakomane naoni, nimunene nao, Ndife akapolo anu; ndipo tsopano mupangane nafe.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 9