Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 8:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndipo ine, ndi anthu onse ali nane, tidzayandikira mudzi; ndipo kudzali, pamene aturuka kudzakomana nafe, monga poyamba paja, tidzathawa pamaso pao;

6. ndipo adzaturuka kutitsata mpaka tidawakokera asiyane ndi mudzi; pakuti adzanena, Atithawa pamaso pathu monga poyamba pala; nafenso tidzathawa pamaso pao;

7. pamenepo muziuka m'molalira ndi kulowa m'mudzi; pakuti Yehova Mulungu wanu adzaupereka m'manja mwanu.

8. Ndipo kudzali, mutagwira mudzi, muzitentha mudziwo ndi moto; muzicita monga mwa mau a Yehova; taonani, ndakulamulirani.

9. Ndipo Yoswa anawatuma, namuka iwo kulowa m'molalira, nakhala pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai; koma Yoswa anakhala mwa anthu usiku uja.

10. Ndipo Yoswa analawira mamawa, nayesa anthu, nakwera, iye ndi akuru a Israyeli, pamaso pa anthu a ku Ai.

11. Ndi anthu onse a nkhondo okhala naye anakwera, nayandikira nafika pamaso pa mudzi, namanga misasa kumpoto kwa Ai; koma pakati pa iye ndi Ai panali cigwa.

12. Ndipo anatenga amuna ngati zikwi zisanu, nawaika m'molalira pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa mudzi.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 8