Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 8:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndipo kunali, atatha Israyeli kupha nzika zonse za ku Ai, kuthengo, kucipululu kumene anawapitikitsira, natha onse kugwa ndi lupanga lakuthwa mpaka adathedwa onse, Aisrayeli onse anabwerera ku Ai, naukantha ndi lupanga lakuthwa.

25. Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.

26. Popeza Yoswa sanabweza dzanja lace limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.

27. Koma ng'ombe ndi zofunkha za mudzi uwu Israyeli anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 8