Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pamene mafumu onse a Aamori okhala tsidya la kumadzulo la Yordano, ndi mafumu onse a Akanani okhala ku Nyanja ya Mcere anamvakuti Yehova anaphwetsa madzi a Yordano pamaso pa ana a Israyeli mpaka titaoloka, mtima wao unasungunuka, analibenso moyo cifukwa ca ana a Israyeli.

2. Nthawi imeneyo Yehova anati kwa Yoswa, Udzisemere mipeni yamiyala, nudulenso ana a Israyeli kaciwiri.

3. Ndipo Yoswa anadzisemera mipeni yamiyala nadula ana a Israyeli pa Gibeya Naraloti.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 5