1. Ndipo kunali, pamene mafumu onse a Aamori okhala tsidya la kumadzulo la Yordano, ndi mafumu onse a Akanani okhala ku Nyanja ya Mcere anamvakuti Yehova anaphwetsa madzi a Yordano pamaso pa ana a Israyeli mpaka titaoloka, mtima wao unasungunuka, analibenso moyo cifukwa ca ana a Israyeli.
2. Nthawi imeneyo Yehova anati kwa Yoswa, Udzisemere mipeni yamiyala, nudulenso ana a Israyeli kaciwiri.
3. Ndipo Yoswa anadzisemera mipeni yamiyala nadula ana a Israyeli pa Gibeya Naraloti.