Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 4:6-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. kuti ici cikhale cizindikilo pakati pa inu. Akakufunsani ana anu m'tsogolomo, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani ndi inu?

7. munene nao, Cifukwa madzi a Yordano anadulidwa patsogolo pa likasa la cipangano ca Yehova; muja lidaoloka Yordano, madzi a Yordano anadulidwa; ndipo miyala iyi idzakhala cikumbutso ca ana a Israyeli cikhalire.

8. Ndipo ana a Israyeli anacita monga Yoswa anawalamulira, nasenza miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordano, monga Yehova adalankhula ndi Yoswa, monga mwa kuwerenga kwa mapfuko a ana a Israyeli; ndipo anaoloka nayo kumka kogona, naiika komweko.

9. Ndipo Yoswa anaimika miyala khumi ndi iwiri pakati pa Yordano, poimapo mapazi a ansembe akusenza likasa la cipangano; ikhala komweko kufikira lero lino.

10. Pakuti ansembe akusenza likasa anaima pakati pa Yordano, mpaka zitatha zonse Yehova adazilamulira Yoswa anene kwa anthu, monga mwa zonse Mose adalamulira Yoswa; ndipo anthu anafulumira kuoloka.

11. Ndipo kunali, atatha kuoloka anthu onse, likasa la Yehova linaoloka, ndi ansembe, pamaso pa anthu.

12. Ndipo ana a Rubeni, ndi ana a Gadi, ndi gawo lija la pfuko la Manase anaoloka ndi zida zao pamaso pa ana a Israyeli, monga Mose adanena nao;

13. ngati zikwi makumi anai ankhondo okonzeka anaoloka pamaso pa Yehova kuthira nkhondo ku zidikha za Yeriko.

14. Tsiku lomwelo Yehova anakulitsa Yoswa pamaso pa Aisrayeli onse; ndipo anamuopa monga anaopa Mose, masiku onse amoyowace.

15. Ndipo Yehova anati kwa Yoswa,

16. Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kuturuka m'Yordano.

17. Pamenepo Yoswa analamulira ansembe, ndi kuti, Kwerani kuturuka m'Yordano.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 4