Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 4:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pamenepo Yoswa anaitana amuna khumi ndi awiriwo amene anawaikiratu mwa ana a Israyeli, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

5. nanena nao Yoswa, Olokani, kutsogolera likasa la Yehova Mulungu wanu pakati pa Yordano, nimudzisenzere yense mwala paphewa pace, monga mwa kuwerenga kwa mapfuko a ana a Israyeli;

6. kuti ici cikhale cizindikilo pakati pa inu. Akakufunsani ana anu m'tsogolomo, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani ndi inu?

7. munene nao, Cifukwa madzi a Yordano anadulidwa patsogolo pa likasa la cipangano ca Yehova; muja lidaoloka Yordano, madzi a Yordano anadulidwa; ndipo miyala iyi idzakhala cikumbutso ca ana a Israyeli cikhalire.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 4