Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 4:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo anthu anakwera kuturuka m'Yordano tsiku lakhumi la mwezi woyamba, namanga misasa ku Giligala, mbali ya ku m'mawa kwa Yeriko.

20. Ndipo Yoswa anaimika ku Giligala miyala ija khumi ndi iwiri adaitenga m'Yordano.

21. Ndipo anati kwa ana a Israyeli, Ana anu akadzafunsa atate ao masiku akudza, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani?

22. pamenepo muzidziwitsa ana anu, ndi kuti, Israyeli anaoloka Yordano uyu pouma.

23. Pakuti Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yordano pamaso panu, mpaka mutaoloka; monga Yehova Mulungu wanu anacitira Nyanja Yofiira, imene anaiphwetsa pamaso pathu, mpaka titaoloka;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 4