Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 4:16-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Lamulira ansembe akusenza likasa la umboni, kuti akwere kuturuka m'Yordano.

17. Pamenepo Yoswa analamulira ansembe, ndi kuti, Kwerani kuturuka m'Yordano.

18. Ndipo kunali, atakwera ansembe akusenza likasa la cipangano la Yehova, kuturuka pakati pa Yordano, nakwera pamtunda mapazi a ansembe, madzi a m'Yordano anabwera m'njira mwace, nasefuka m'magombe ace onse monga kale.

19. Ndipo anthu anakwera kuturuka m'Yordano tsiku lakhumi la mwezi woyamba, namanga misasa ku Giligala, mbali ya ku m'mawa kwa Yeriko.

20. Ndipo Yoswa anaimika ku Giligala miyala ija khumi ndi iwiri adaitenga m'Yordano.

21. Ndipo anati kwa ana a Israyeli, Ana anu akadzafunsa atate ao masiku akudza, ndi kuti, Miyala iyi nja ciani?

22. pamenepo muzidziwitsa ana anu, ndi kuti, Israyeli anaoloka Yordano uyu pouma.

23. Pakuti Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yordano pamaso panu, mpaka mutaoloka; monga Yehova Mulungu wanu anacitira Nyanja Yofiira, imene anaiphwetsa pamaso pathu, mpaka titaoloka;

24. kuti mitundu yonse ya pa dziko lapansi idziwe dzanja la Yehova, kuti ndilo lamphamvu; kuti lope Yehova Mulungu wanu masiku onse.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 4