Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 24:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. ndipo Yehova anaingitsa pamaso pathu anthu awa onse, ngakhale Aamori okhala m'dzikomo; cifukwa cace ifenso tidzatumikira Yehova, pakuti ndiye Mulungu wathu.

19. Ndipo Yoswa anati kwa anthu, Simukhoza inu kutumikira Yehova pakuti ndiye Mulungu woyera, ndi Mulungu wansanje; sadzalekerera zolakwa zanu, kapena zocimwa zanu.

20. Mukasiya Yehova, ndi kutumikira milungu yacilendo, adzatembenuka ndi kukucitirani coipa, ndi kukuthani, angakhale anakucitirani cokoma.

21. Ndipo anthu anati kwa Yoswa, Iaitu, koma tidzatumikira Yehova.

22. Ndipo Yoswa ananena ndi anthu, Inu mwadzicitira mboni inu nokha kuti mwadzisankhira Yehova kumtumikira iye. Ndipo anati, Ndife mboni.

23. Ndipo tsopano, cotsani milungu yacilendo iri pakati pa inu, ndi kulozetsa mitima yanu kwa Yehova, Mulungu wa Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 24