Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 24:15-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo ngati kutumikira Yehova kukuipirani mudzisankhire lero amene mudzamtumikira, kapena milungu imene anaitumikira makolo anu okhala tsidya lija la mtsinje, kapena milungu ya Aamori amene mukhala m'dziko lao; koma ine, ndi a m'nyumba yanga, tidzatumikira Yehova.

16. Ndipo anthu anayankha, nati, Sikungatheke kuti timsiye Yehova, ndi kutumikira milungu yina;

17. pakuti Yehova Mulungu wathu ndi iye amene anatikweza kutiturutsa m'dziko la Aigupto ku nyumba ya akapolo, nacita zodabwiza zazikuruzo pamaso pathu, natisunga m'njira monse tidayendamo, ndi pakati pa anthu onse amene tinapita pakati pao;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 24