Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 22:2-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. nanena nao, Mwasunga inu zonsezo anakulamulirani Mosemtumiki wa Yehova; mwamveranso mau anga m'zonse ndinakulamulirani inu;

3. simunasiya abale anu masiku awa ambiri mpaka lero lino, koma mwasunga cisungire lamulola Yehova Mulungu wanu.

4. Ndipo tsopano Yehova Mulungu wanu wapumitsa abale anu, monga adanena nao; potero bwererani tsopano, mu kani ku mahema anu, ku dziko la colowa canu cimene Mose mtumiki wa Yehova anakuninkhani tsidya lija la Yordano.

5. Koma samalirani bwino kuti mucite cilangizo ndi cilamulo zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulirani kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace zonse ndi kusunga malamulo ace, ndi kumuumirira iye, ndi kumtumikira iye ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.

6. Momwemo Yoswa anawadalitsa, nawauza amuke; ndipo anamuka ku mahema ao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 22