21. Ndipo anawapatsa Sekemu ndi mabusa ace ku mapiri a Efraimu, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo, ndi Gezeri ndi mabusa ace;
22. ndi Kibizaimu ndi mabusa ace, Betihoroni ndi mabusa ace; midzi inai.
23. Ndipo motapira m'pfuko La Dani, Eliteke ndi mabusa ace, Gibetoni ndi mabusa ace;
24. Aijaloni ndi mabusa ace, Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi inai.
25. Ndipo motapira pa pfukola Manaselogawika pakati, Taanaki ndi mabusa ace, ndi Gati-rimoni ndi mabusa ace; midzi iwiri.
26. Midzi yonse ya mabanja a ana otsala a Kohati ndiyo khumi ndi mabusa ao.
27. Ndipo anapatsa ana a Gerisoni, a mabanja a Alevi, motapira pa pfuko la Manase logawika pakati, Golani m'Basana ndi mabusa ace, ndiwo mudzi wopulumukirako wakupha mnzaceyo; ndi Beesitera ndi mabusa ace; midzi iwiri.
28. Ndipo motapira pa pfuko la Isakara, Kisioni ndi mabusa ace, Daberati ndi mabusa ace;
29. Yarimutu ndi mabusa ace, Eniganimu ndi mabusa ace; midzi inai.
30. Ndipo motapira pa pfuko La Aseri, Misali ndi mabusa ace, Abidoni ndi mabusa ace;
31. Helikati ndi mabusa ace, ndi Rehobo ndi mabusa ace; midzi inai.