Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 2:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo amunawo anawalondola pa njira ya ku Yordano yomka kudooko; ndipo ataturuka akuwalondola, anatseka pacipata.

8. Koma asanagone iwo, anawakwerera patsindwi iye,

9. nati kwa amunawo, Ndidziwa kuti Yehova wakupatsani dzikoli, ndi kuti kuopsa kwanu kwatigwera, ndi kuti okhala m'dziko onse asungunuka pamaso panu.

10. Popeza tidamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a m'Nyanja Yofiira pamaso panu, muja mudaruruka m'Aigupto; ndi cija munacitira mafumu awiri a Aamori okhala tsidya la Yordano, ndiwo Sihoni ndi Ogi, amene mudawaononga konse.

11. Ndipo titamva ici mitima yathu inasungunuka; anahbenso mtima ndi mmodzi yense, cifukwa ca inu; pakuti Yehova Mulungu wanu, ndiye Mulungu wa m'mwamba umo, ndi pa dziko lapansi.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 2