Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 2:11-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo titamva ici mitima yathu inasungunuka; anahbenso mtima ndi mmodzi yense, cifukwa ca inu; pakuti Yehova Mulungu wanu, ndiye Mulungu wa m'mwamba umo, ndi pa dziko lapansi.

12. Ndipo tsopano, mundilumbiriretu kwa Yehova, popeza ndakucitirani cifundo, kuti inunso mudzacitira cifundo a m'nyumba ya atate wanga ndi kundipatsa cizindikilo coona,

13. kuti mudzawasunga ndi moyo atate wanga ndi mai wanga, ndi alongo anga ndi abale anga, ndi zonse ali nazo, ndi kupulumutsa miyoyo yathu kuimfa.

14. Ndipo amunawo anati kwa iye, Moyo wathu ndiwo moyo wanu, mukapanda kuulula codzera ife; ndipo kudzakhala kuti, pakutipatsa ife dziko ili Yehova, tidzakucitira cifundo ndi coonadi.

15. Pamenepo anawatsitsa pazenera ndi cingwe; popeza nyumba yace lnali pa linga La mudzi, nakhala iye palingapo.

16. Ndipo anati kwa iwo, Mukani kuphiri, olondola angakupezeni; mubisale kumeneko masiku atatu, mpaka atabwerera olondolawo, pamenepo muyende ulendo wanu.

17. Ndipo amunawo anati kwa iye, Sitidzacimwira lumbiro lako ili watilumbiritsali.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 2