Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 19:14-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;

15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.

16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

22. ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.

23. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

24. Ndipo maece acisanu analiturukira pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao.

25. Ndi malire ao ndiwo Helikati, ndi Hali, ndi Beteni ndi Akisafu;

26. ndi Alameleki, ndi Amadi, ndi Misali; nafikira ku Karimeli kumadzulo ndi ku Sihorilibinati;

27. nazungulira koturukira dzuwa ku Beti-dagoni, nafikira ku Zebuloni ndi ku cigwa ca Ifita-eli, kumpoto ku Beti-emeki, ndi Nehieli; naturukira ku Kabulu kulamanzere,

Werengani mutu wathunthu Yoswa 19