Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 19:10-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo maere acitatu anakwecera ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao; ndi malire a colowa cao anafikira ku Saridi;

11. nakwera malire ao kumka kumadzulo ndi ku Marala nafikira ku Dabeseti, nafikira ku mtsinje wa patsogolo pa Yokineamu;

12. ndi kucokera ku Saridi anazungulira kumka kum'mawa kumaturukira dzuwa, mpaka malire a Kisilotu-tabori; naturuka kumka ku Daberati, nakwera ku Yafia;

13. ndi pocoka pamenepo anapitirira kumka kum'mawa ku Gati-heferi, ku Etikazini; naturuka ku Remoni umene ulembedwa mpaka ku Nea,

14. nauzungulira malire kumpoto, kumka ku Hanatoni; ndi maturukiro ace anali ku cigwa ca Ifita-eli;

15. ndi Kata, ndi Nahalala ndi Simironi, ndi Idala ndi Betelehemu: midzi khumi ndi iwiri ndi miraga yao.

16. Ici ndi colowa ca ana a Zebuloni monga mwa mabanja ao, midzi iyi ndi miraga yao.

17. Maere acinai anamturukira Isakara, kunena za ana a Isakara monga mwa mabanja ao.

18. Ndi malire ao anali ku Yezireeli, ndi Kesulotu, ndi Sunemu;

19. ndi Hafaraimu, ndi Sioni, ndi Anaharati;

20. ndi Rabiti ndi Kisioni, ndi Ebezi;

21. ndi Remeti ndi Eni-ganaimu ndi Eni-hada, ndi Beti-Pazezi;

22. ndi malire anafikira ku Tabori, ndi Sahazuma, ndi Betesemesi; ndi maturukiro a malire ao anali ku Yordano; midzi khumi ndi isanu ndi umodzi ndi miraga yao.

23. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Isakara, monga mwa mabanja ao, midzi ndi miraga yao.

24. Ndipo maece acisanu analiturukira pfuko la ana a Aseri monga mwa mabanja ao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 19