Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:17-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. nalembedwa kumka kumpoto, naturuka ku Eni-semesi, naturuka ku Gelilotu, ndiwo pandunji pokwerera pa Adumi; natsikira ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

18. napitirira ku mbali ya pandunji pa Araba kumpoto, natsikira kumka ku Araba;

19. napitirira malire kumka ku mbali ya Beti-hogila kumpoto; ndi maturukiro ace a malire anali ku nyondo ya kumpoto ya Nyanja ya Mcere; pa kulekezera kwa kumwela kwa Yordano; ndiwo malire a kumwera.

20. Ndipo malireace mbali ya kum'mawa ndiwo Yordano, ndico colowa ca ana a Benjamini, kunena za malire ace pozungulira pace, monga mwa mabanja ao.

21. Koma midzi ya pfuko la ana a Benjamini monga mwa mabanja ao ndiyo Yeriko, ndi Beti-hogila, ndi Emekikozizi;

22. ndi Beti-araba, ndi Zemaraimu, ndi Beteli;

23. ndi Arimu ndi Para, ndi Ofira;

24. ndi Kefaraamoni, ndi Ofini, ndi Geba; midzi khumi ndi iwiri pamodzi ndi miraga yao;

25. Gibeoni ndi Rama, ndi Beeroti;

26. ndi Mizipe, ndi Kefira, ndi Moza;

27. ndi Rekemu, ndi Iripeeli ndi Tarala;

28. ndi Zela, Elefi, ndi Yebusi, womwewo ndi Yerusalemu, Gibeati ndi Kiriyati; midzi khumi ndi inai pamodzi ndi miraga yace, Ndico colowa ca ana a Benjamini monga mwa mabanja ao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18