Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:13-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo malire anapitirirapo kumka ku Luzi, ku mbali ya Luzi, momwemo ndi Beteli, kumwela; ndi malire anatsikira kumka ku Atarotu-adara, ku phiri lokhala kumwela kwa Betihoroni wa kunsi.

14. Ndipo malire analembedwa nazungulira ku mbali ya kumadzulo kumka kumwela, kucokera ku phiri pokhala patsogolo pa Beti-horoni, kumwela kwace; ndi maturukiro ace anali ku Kiriyatibaala, womwewo ndi Kiriyati-Yearimu, mudzi wa ana a Yuda; ndiyo mbali ya kumadzulo.

15. Ndipo mbali ya kumwela inayambira polekezera Kiriyati-Yearimu; naturuka malire kumka kumadzulo, naturuka kumka ku citsime ca madzi a Nefitoa;

16. natsikira malire kumka polekezera phiri lokhala patsogolo pa cigwa ca mwana wa Hinomu, ndico ca m'cigwa ca Refai kumpoto; natsikira ku cigwa ca Hinomu, ku mbali ya Ayebusi kumwela, natsikira ku Enirogeli;

17. nalembedwa kumka kumpoto, naturuka ku Eni-semesi, naturuka ku Gelilotu, ndiwo pandunji pokwerera pa Adumi; natsikira ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

18. napitirira ku mbali ya pandunji pa Araba kumpoto, natsikira kumka ku Araba;

19. napitirira malire kumka ku mbali ya Beti-hogila kumpoto; ndi maturukiro ace a malire anali ku nyondo ya kumpoto ya Nyanja ya Mcere; pa kulekezera kwa kumwela kwa Yordano; ndiwo malire a kumwera.

20. Ndipo malireace mbali ya kum'mawa ndiwo Yordano, ndico colowa ca ana a Benjamini, kunena za malire ace pozungulira pace, monga mwa mabanja ao.

21. Koma midzi ya pfuko la ana a Benjamini monga mwa mabanja ao ndiyo Yeriko, ndi Beti-hogila, ndi Emekikozizi;

22. ndi Beti-araba, ndi Zemaraimu, ndi Beteli;

23. ndi Arimu ndi Para, ndi Ofira;

24. ndi Kefaraamoni, ndi Ofini, ndi Geba; midzi khumi ndi iwiri pamodzi ndi miraga yao;

25. Gibeoni ndi Rama, ndi Beeroti;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18