Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 18:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo malire anapitirirapo kumka ku Luzi, ku mbali ya Luzi, momwemo ndi Beteli, kumwela; ndi malire anatsikira kumka ku Atarotu-adara, ku phiri lokhala kumwela kwa Betihoroni wa kunsi.

14. Ndipo malire analembedwa nazungulira ku mbali ya kumadzulo kumka kumwela, kucokera ku phiri pokhala patsogolo pa Beti-horoni, kumwela kwace; ndi maturukiro ace anali ku Kiriyatibaala, womwewo ndi Kiriyati-Yearimu, mudzi wa ana a Yuda; ndiyo mbali ya kumadzulo.

15. Ndipo mbali ya kumwela inayambira polekezera Kiriyati-Yearimu; naturuka malire kumka kumadzulo, naturuka kumka ku citsime ca madzi a Nefitoa;

16. natsikira malire kumka polekezera phiri lokhala patsogolo pa cigwa ca mwana wa Hinomu, ndico ca m'cigwa ca Refai kumpoto; natsikira ku cigwa ca Hinomu, ku mbali ya Ayebusi kumwela, natsikira ku Enirogeli;

17. nalembedwa kumka kumpoto, naturuka ku Eni-semesi, naturuka ku Gelilotu, ndiwo pandunji pokwerera pa Adumi; natsikira ku mwala wa Bohani mwana wa Rubeni;

18. napitirira ku mbali ya pandunji pa Araba kumpoto, natsikira kumka ku Araba;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 18