Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 17:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anamgwera Manase magawo khumi, osawerenga dziko la Gileadi ndi Basana lokhala tsidya lija la Yordano:

6. popeza ana akazi a Manase adalandira colowa pakati pa ana ace amuna; ndi dziko la Gileadi linakhala la ana a Manase otsala.

7. Ndipo malire a Manase anayambira ku Aseri, kumka ku Mika-metatu, wokhala cakuno ca Sekemu; namuka malire ku dzanja lamanja kwa nzika za Enitapua.

8. Dziko la Tapua linali la Manase; koma Tapua mpaka malire a Manase linakhala la ana a Efraimu.

9. Natsikira malire ku mtsinje wa Kana, kumwera kwa mtsinje; midzi iyi inakhala ya Efraimu pakati pa midzi ya Manase; ndi malire a Manase anali kumpoto kwa mtsinje; ndimaturukiro ace anali kunyanja;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 17