Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 16:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. natsika kucokera ku Yanoa, kumka ku Atarotu, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, naturuka ku Yordano.

8. Kuyambira ku Tapua malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi maturukiro ace anali kunyanja. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Efraimu monga mwa mabanja ao;

9. pamodzi ndi midzi adaipatulira ana a Efraimu pakati pa colowa ca ana a Manase, midzi yonse pamodzi ndi miraga yao.

10. Ndipo a sanaingitsa Akanani akukhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala pakati pa Efraimu, kufikira lero lino, nawasonkhera msonkho.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 16