Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 13:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pamodzi ndi iye Arubeni ndi Agadi analandira colowa cao, cimene Mose adawapatsa tsidya ilo la Yordano kum'mawa, monga Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa;

9. kuyambira pa Aroeri, wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uti pakati pa cigwa, ndi cidikha conse ca Medeba mpaka ku Diboni;

10. ndi midzi yonse ya Sihoni mfumu ya Aamori, wakucita ufumu m'Hesiboni, mpaka malire a ana a Amoni;

11. ndi Gileadi, ndi malire a Agesuri, ndi Amaakati, ndi phiri lonse la Herimoni, ndi Basana ionse mpaka ku Saleka;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 13