8. Pamodzi ndi iye Arubeni ndi Agadi analandira colowa cao, cimene Mose adawapatsa tsidya ilo la Yordano kum'mawa, monga Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa;
9. kuyambira pa Aroeri, wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uti pakati pa cigwa, ndi cidikha conse ca Medeba mpaka ku Diboni;
10. ndi midzi yonse ya Sihoni mfumu ya Aamori, wakucita ufumu m'Hesiboni, mpaka malire a ana a Amoni;
11. ndi Gileadi, ndi malire a Agesuri, ndi Amaakati, ndi phiri lonse la Herimoni, ndi Basana ionse mpaka ku Saleka;