Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 13:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma ana a Israyeli sanainga Agesuri kapena Amaakati; koma Gesuri, ndi Maakati amakhala pakati pa Israyeli, mpaka lero lino.

14. Koma pfuko la Levi sanalipatsa colowa; nsembe za Yehova Mulungu wa Israyeli, zocitika ndi moto, ndizo colowa cace, monga iye adanena naye.

15. Ndipo Mose anapatsira pfuko la ana a Rubeni monga mwa mabanja ao.

16. Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;

17. Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;

18. ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;

19. ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 13