Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 13:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yoswa anakalamba, wa zaka zambiri; ndipo Yehova ananena naye, Wakalamba, wa zaka zambiri, ndipo latsala dziko lalikurukuru, alilandire colowa cao,

2. Dziko lotsala ndilo: malire onse a Afilisti, ndi Agesuri onse,

3. kuyambira Sihoro wokhala cakuno ca Aigupto mpaka malire a Ekironu kumpoto, loyesedwa la Akanani; akalonga asanu a Afilisti, a ku Gaza, ndi a ku Asidodi, a ku Asekelo, a ku Giti, ndi a ku Ekiro, ndi Ahivi;

4. kumwela dziko lonse la Akanani, ndi Meara ndiwo wa Asidoni, mpaka ku Afeka, mpaka ku malire a Aaroori;

Werengani mutu wathunthu Yoswa 13