Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yona 3:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yona nthawi yaciwiri, ndi kuti,

2. Nyamuka, pita ku Nineve mudzi waukuru uja, nuulalikire uthenga umene ndikuuza.

3. Ndipo Yona ananyamuka, napita ku Nineve, monga mwa mau a Yehova. Koma Nineve ndiwo mudzi waukuru pamaso pa Yehova, wa ulendo wa masiku atatu.

4. Ndipo Yona anayamba kulowa mudziwo ulendo wa tsiku limodzi, nalalikira, nati, Atsala masiku makumi anai ndipo Nineve adzapasuka.

5. Ndipo anthu a Nineve anakhulupirira Mulungu, nalalikira cosala, nabvala ciguduli, kuyambira wamkuru kufikira wamng'ono wa iwowa.

Werengani mutu wathunthu Yona 3