Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yona 1:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. NDIPO mau a Yehova anadza kwa Yona mwana wa Amitai, ndi kuti,

2. Nyamuka, pita ku Nineve, mudzi waukuruwo, nulalikire motsutsana nao; pakuti coipa cao candikwerera pamaso panga.

3. Koma Yona ananyamuka kuti athawire ku Tarisi, kuzemba Yehova; ndipo anatsikira ku Yopa, napezako combo comuka ku Tarisi, napereka ndalama zace, natsikira m'menemo, kuti apite nao ku Tarisi kuzemba Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yona 1