Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 42:4-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Tamveranitu, ndidzanena ine,Ndidzakufunsani, mundidziwitse.

5. Kumva ndidamva mbiri yanu,Koma tsopano ndikupenyani maso;

6. Cifukwa cace ndekha ndidzinyansa, ndi kulapaM'pfumbi ndi mapulusa.

7. Kunali tsono atanena Yehova mau awa kwa Yobu, Yehova anati kwa Elifazi wa ku Temani, Mkwiyo wanga wakuyakira iwe ndi mabwenzi ako awiri, pakuti simunandinenera coyenera monga ananena mtumiki wanga Yobu.

8. Ndipo tsono, mudzitengere ng'ombe zisanu ndi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri, mumuke kwa mtumiki wanga Yobu, mudzifukizire nokha nsembe yopsereza; ndi mtumiki wanga Yobu adzapempherera inu, pakuti ndidzambvomereza iyeyu, kuti ndisacite nanu monga mwa kupusa kwanu; popeza simunandinenera coyenera monga ananena mtumiki Yobu.

9. Namuka Elifazi wa ku Temani, ndi Bilidadi Msuki, ndi Zofara wa ku Naama, nacita monga Yehova adawauza; ndipo Yehova anabvomereza Yobu.

10. Ndipo Yehova anacotsa ukapolo wa Yobu, pamene anapempherera mabwenzi ace; Yehova nacurukitsa zace zonse za Yobu mpaka kuziwirikiza.

11. Pamenepo anamdzera abale ace onse, ndi alongo ace onse, ndi onse odziwana naye kale, nadya naye mkate m'nyumba yace, nampukusira mitu, namtonthoza pa zoipa zonse Yehova anamfikitsirazi; nampatsanso yense ndarama ndi mphete yagolidi.

12. Ndipo Yehova anadalitsa citsiriziro ca Yobu koposa ciyambi cace, ndipo anali nazo nkhosa zikwi khumi ndi zinai, ndi ngamila zikwi zisanu ndi cimodzi, ndi ng'ombe zamagoli cikwi cimodzi, ndi aburu akazi cikwi cimodzi.

13. Anali naonso ana amuna asanu ndi awiri ndi ana akazi atatu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 42