Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 42:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndidziwa kuti mukhoza kucita zonse,Ndi kuti palibe coletsa colingirira canu ciri conse,

3. Ndani uyu abisa uphungu wosadziwa kanthu?Cifukwa cace ndinafotokozera zimene sindinazizindikira,Zondidabwiza, zosazidziwa ine,

4. Tamveranitu, ndidzanena ine,Ndidzakufunsani, mundidziwitse.

5. Kumva ndidamva mbiri yanu,Koma tsopano ndikupenyani maso;

6. Cifukwa cace ndekha ndidzinyansa, ndi kulapaM'pfumbi ndi mapulusa.

7. Kunali tsono atanena Yehova mau awa kwa Yobu, Yehova anati kwa Elifazi wa ku Temani, Mkwiyo wanga wakuyakira iwe ndi mabwenzi ako awiri, pakuti simunandinenera coyenera monga ananena mtumiki wanga Yobu.

Werengani mutu wathunthu Yobu 42