Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 35:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Yang'anani kumwamba, nimuone,Tapenyani mitambo yokwera yakuposa inu.

6. Ngati mwacimwa, mumcitira Iye ciani?Zikacuruka zolakwa zanu, mumcitira Iye ciani?

7. Mukakhala wolungama, mumninkhapo ciani?Kapena alandira ciani pa dzanja lanu?

8. Coipa canu cikhoza kuipira munthu wonga inu,Ndi cilungamo canu cikhoza kukomera wobadwa ndi munthu.

9. Cifukwa ca kucuruka masautso anthu anapfuula,Apfuula cifukwa ca dzanja la amphamvu.

10. Koma palibe anganene, Ali kuti Mulungu Mlengi wanga,Wakupatsa nyimbo usiku;

11. Wakutilangiza ife koposa nyama za padziko,Wakutipatsa nzeru zoposa mbalame za m'mlengalenga?

Werengani mutu wathunthu Yobu 35