Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 35:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti munena, Upindulanji naco?Posacimwa ndinapindula ciani cimene sindikadapindula pocimwa?

4. Ndidzakuyankhani,Ndi anzanu pamodzi ndi inu.

5. Yang'anani kumwamba, nimuone,Tapenyani mitambo yokwera yakuposa inu.

6. Ngati mwacimwa, mumcitira Iye ciani?Zikacuruka zolakwa zanu, mumcitira Iye ciani?

7. Mukakhala wolungama, mumninkhapo ciani?Kapena alandira ciani pa dzanja lanu?

8. Coipa canu cikhoza kuipira munthu wonga inu,Ndi cilungamo canu cikhoza kukomera wobadwa ndi munthu.

9. Cifukwa ca kucuruka masautso anthu anapfuula,Apfuula cifukwa ca dzanja la amphamvu.

10. Koma palibe anganene, Ali kuti Mulungu Mlengi wanga,Wakupatsa nyimbo usiku;

Werengani mutu wathunthu Yobu 35